Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 138

Paphata pa Chichewa Kukankhira kunkhongo: Kusiya kuganizira nkhani ina- yake, kunyalanyaza nkhani. Chitsanzo: Musavutike nayo mtima nkhani imeneyi, in- goikankhirani kunkhongo. Kukantha: Kumenya. Chitsanzo: Amukantha ndi chikuni. Kukaswa miyala: Kukachita chimbudzi kapena kukabiba. Chitsanzo: Angozungulira kuseriku, mwina apita kokaswa miyala. Akanakhala akukataya madzi bwenzi atabwerako kalekale. Kukata: Kusiya, kutha. Amagwiritsidwanso ntchito aka- manena zoti mvula yasiya kapena ikusiya. Chitsanzo: Matenda pakhomo pano sakukata. Kukatamuka: Kupeza ndalama zambiri. Chitsanzo: (1) Mbala ngakhale aimenye, sivomera kuti yaba ndalama chifukwa imadziwa kuti akangoimasula si kukatamuka kwakeko! (2) Akungomwaza ndalama. Zikuoneka kuti wakatamuka. Kukazinga mowa: Kutcheza kapena kuphika mowa wokoma. Chitsanzo: Koma ndiye mwaukazingatu mowawu. Kukhala limodzi: Kugonana. Chitsanzo: (1) Zimakhala zochititsa manyazi kumakhala limodzi ndi mtsikana musanakwatirane. (2) Zikuoneka kuti anakhalapo limodzi. Kukhala m’maluzi: Kukhala opanda ndalama. Chitsanzo: Anthu ambiri ali m’maluzi. 137