Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 137
Paphata pa Chichewa
Kukamulowerera mwamuna: Mawuwa amaneneda mtsi-
kana akathawa kwawo n’kupita kumakakhala ndi
mwamuna ukwati usanachitike.
Chitsanzo: Mtsikana wofatsa uja anakamulowerera
mwamuna.
Kukana kali kutsaya: Kukana ukudziwa kuti wachita
ndiwe, kukana pali umboni woti wachita ndiwe.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani ukukana kali kutsaya?
Kukana kali kutsaya: Kukana ukudziwa kuti zimene
akukufunsazo ndi zoona.
Chitsanzo: (1) Bambowa akukana kali kutsaya. (2) Ata-
mupezerera akuvuula ndiwo mumphika, anamufunsa kuti
akutani, koma iye anayamba kukana kali kutsaya.
Kukana kwam’tuwagalu: Kukanitsitsa.
Chitsanzo: (1) Nditamupempha kuti andithandize
kunyamula thumbalo, anandikanira kwam’tuwagalu. (2)
Atamufunsa anakana kwam’tuwagalu.
Kukang’antha:
(a) Kumenya.
Chitsanzo: Anamukang’antha ndi mtengo.
(b) Kuvutika kwambiri, kusowa ndalama.
Chitsanzo: Maluzi amukang’antha.
Kukanjuta: Kukabiba, kukanyera.
Chitsanzo: Alowa pachikangapo akukanjuta.
Kukankha chikopa: Kudziwa kumenya mpira wa
miyendo.
Chitsanzo: Mwanayu amakankha chikopa.
136