Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 133
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Mwana wawo uja amamuhonga. (2) Anapita
kukahonga kuti aziwanda.
Kuijangirira: Kuchita zinthu mwadongosolo.
Chitsanzo: Mukaijangirira nyumba imeneyi idzaoneka
bwino.
Kuika pamoto: Kuika pamavuto.
Chitsanzo: Mukapanda kumuthandiza mwana wanuyu
akuikani pamoto.
Kuika: Kukwirira m’manda.
Chitsanzo: Maliro aja anaika.
Kuikirapo mtima: Kulimbikira.
Chitsanzo: Anapambana chifukwa anaikapo mtima.
Kuilumira mano: Kuichitira khama.
Chitsanzo: Ntchito imeneyi kuilumira mano
ingadzakupezetseni ndalama zambiri.
Kuima mitu: Kusowa chochita.
Chitsanzo: Nkhani imeneyi yandiimitsa mutu.
Kuima: Kukhala ndi pakati.
Chitsanzo: Mayi akaima, sayenera kumavala mabuluku.
Kuimba lokoma: Kusangalala.
Chitsanzo: Mphaka akachoka, khoswe amaimba lokoma.
Kuimba sukulu: Kuphunzira sukulu.
Chitsanzo: Ife sitinaimbe sukulu.
Kuimika makutu: Kutchera khutu.
Chitsanzo: Musanene chilichonse, anthu onse aimika ma-
kutu!
132