Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 132

Paphata pa Chichewa Kugwira nsewu: Kuyamba kuyenda bwino, kuzolowera kuchita zinazake. Chitsanzo: (1) Patenga nyengo kuti munthu ameneyu ag- wire nsewu. (2) Ulimi wawo unagwira nsewu. Kugwira nthawi: Kubwera kapena kuchita zinthu pa nthawi yake. Chitsanzo: (1) Aliyense adzagwire nthawi. (2) Amalawi zimawavuta kugwira nthawi. (3) Ameneyu ndi munthu wogwira nthawi. Kugwira tambala kukamwa: Kulawirira. Chitsanzo: Kuti tikafike nthawi yabwino, mpofunika tigwire tambala kukamwa. Kugwira: Kuyamba chibwenzi. Chitsanzo: Wagwira kanjole kapamtundapo. Kugwiririra: Kukakamiza munthu kuti ugone naye. Chitsanzo: (1) Njonda ina imafuna kumugwiririra. (2) Anasokonekera chifukwa anthu anamugwiririra ali mwa- na. Kugwiritsa kenakake: Kupatsa munthu ndalama kapena zinthu zina. Chitsanzo: (1) Bwerani mundithandize, ndikugwiritsani kenakake. (2) Ayenera kukugwiritsa kenakake, simungangogwira ulere! Kuhonga: Kunyengerera munthu kuti achite zinazake. Chitsanzo: Anthu ena amafuna kuwahonga kaye kuti akuthandize kugwira ntchito. Kuhonga: Kunyengerera munthu pomuchitira zabwino kapena kumuchitira zinazake. 131