Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 131
Paphata pa Chichewa
Kugwetsa nkhope: Kuchita manyazi.
Chitsanzo: Pamene mwanayo amaulula zonse, bambowo
anagwetsa nkhope.
Kugwetsa:
(a) Kutaya chinthu pansi mwadala kapena ayi.
Chitsanzo: (1) Agwetsa foni. (2) Wagwetsa nyumba.
(b) Kumaliza.
Chitsanzo: (1) Tiyeni tigwetse ntchito. (2) Wagwetsa
makapu awiri a mowa.
Kugwidwa: Kukhala pachibwenzi, kufunsiridwa.
Chitsanzo: Mtsikana ameneyutu anagwidwa kale, un-
gawononge nthawi!
Kugwintha: Mawu okokomeza komanso achipongwe
onyoza munthu amene akudya.
Chitsanzo: (1) Anawa safuna kugwira ntchito koma
kugwintha. (2) Tazingogwinthani apa!
Kugwira dzanja (nkono): Kuthandiza.
Chitsanzo: Amenewa ndi amene anandigwira dzanja
zinthu zitandivuta.
Kugwira dzanja: Kuthandiza
Chitsanzo: Sumachitira mwano munthu amene
anakugwira dzanja.
Kugwira mwendo: Kuchonderera, kupempha mochon-
derera, kupepesa posonyeza kugonja.
Chitsanzo: (1) Ndagwira mwendo wanu, ndithandizeni
chonde! (2) Musandithamangitse bwana, ndagwira
mwendo wanu!
130