Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 130

Paphata pa Chichewa Kugwa mphwayi: Kufooka. Chitsanzo: Musagwe mphwayi, mukhoza kupambana. Kugwa nkhope: Kuchita manyazi chifukwa chodzudzu- lidwa. Chitsanzo: Ukamadzudzula mtsikana woyendayenda, sa- magwa nkhope, koma amakutembenukira n’kuyamba ku- kusambwadza. Kugwa ulesi: Kufooka, kugwa mphwayi, kutaya mtima, Kusiya kukopeka ndi chinthu. Chitsanzo: (1) Nkhaniyi yandigwetsa ulesi. (2) Ndagwa ulesi, basi sindipitakonso. (3) Nditazindikira kuti ndalephera mayeso, ndinangogwa ulesi n’kuisiya sukulu. Kugwa ulesi: Kufooka, kusiya kulimbikira. Chitsanzo: Zimene anenazi ndi zimene zatigwetsa ulesi. Kugwaza: Kupha mochita kubaya kapena kutema. Chitsanzo: Akugwaza mkango m’thengomo. Kugwedezeka (kutekeseka): Mawuwa amanenedwa zika- khala kuti nkhani imene ili m’kamwam’kamwa ndi ya munthu winawake, aliyense akungokamba za iye. Anga- tanthauzenso kuti zinthu zinasinthiratu munthuyo atan- gobwera. Chitsanzo: Atangofika mudzi wonse unagwedezeka. Kugwera: Kuchita zinazake mwamwayi. Chitsanzo: Sikuti amandiposa bawo, lerolo wangogwera. Kugwetsa misozi: Kulira. Chitsanzo: Ndinalephera kudzigwira moti ndinagwetsa misozi. 129