Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 13
Paphata pa Chichewa
Atate:
(a) Munthu wolemekezeka.
Chitsanzo: Amenewa ndiye atate a pankhani zoimbaimba.
(b) Bambo.
Chitsanzo: Atate awo abwera mawa.
Atengerepo phunziro: Aphunzirepo kanthu.
Chitsanzo: Ndakhaulitsa enawa kuti enawo atengerepo
phunziro.
Athakati (nthakati): Afiti.
Chitsanzo: M’mudzi muno mwachuluka athakati.
Athupi: Wonenepa.
Chitsanzo: Abale awo onse ndi athupi.
Atisiya: Amwalira.
Chitsanzo: Munthu amadwala uja watisiya.
Atsibweni: Amalume, alongo awo a mayi.
Chitsanzo: Kwabwera atsibweni anga.
Auyamba ulendo: Anyamuka apita.
Chitsanzo: Anzathu onse auyamba ulendo.
Awachesula: Mawuwa amanenedwa ndi anthu omwe
amakhulupirira za ufiti kuti wina walodza mnzake.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani ukuchita makani?
Akuchesula eti!
Awadyetsa chibanzi: Awatseka pakamwa kuti
asayankhule powapatsa chiphuphu.
Chitsanzo: Zikuoneka kuti wolakwayo wawadyetsa
chibanzi apolisiwo.
12