Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 127

Paphata pa Chichewa Kugomera: Kusirira munthu kapena chinachake. Chitsanzo: Ndimamugomera mnyamata amene uja. Kugona (kugonana): Kuchita chiwerewere. Chitsanzo: (1) Ngati ukufuna kuti matenda a bomawa akuphonye, umafunika kupewa kumangogona ndi ali- yense. (2) Munthu wanzeru samangogonana ndi aliyense. Kugona mphika wapserera: Kugona pang’ono chifukwa cha kanthu kena. Chitsanzo: Timadikirira alendo moti lero tagona mphika wapserera. Kugona mutu uli kukhomo: Kugona mofunitsitsa kuti kuche msanga. Chitsanzo: Anthu onse omwe amapita kukagula chimanga adagona mutu uli kukhomo. Kugona ngati mvuu: Kugona mosalongosoka. Chitsanzo: Achimwene anu amagona ngati mvuu. Akagona ataloza uku, amadzuka ataloza kwinako. Kugona tulo tofa nato: Kugona tulo tatikulu. Chitsanzo: Ndi kale ndinagona tulo tofa nato. Kugonekera khosi (kuthyolera khosi): Kusonyeza kuti ukugwirizana nazo. Chitsanzo: (1) Akayamba kunena zake zija osamugonekera khosi. (2) Mtsikana akagonekera khosi amakhala kuti wakulola. Kugonekera khosi: Kuvomereza zimene wina akufuna. Chitsanzo: (1) Ukamangogonekera khosi munthu aliyense, ukumana ndi mavuto. (2) Amangogonekera khosi mnya- mata aliyense. 126