Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 123

Paphata pa Chichewa Kufera m’khwapa: Kukanikiratu kuchita chinthu monga kuyankhula. Chitsanzo: Pamlanduwo, wolakwayo sanayankhe chilichonse moti anangofera m’khwapa. Kufewa m’manja: Kupatsa. Chitsanzo: Ukakhala wofewa manja, anthu amakuzolow- era. Kufika pamtima: Kukhudza mtima, kusangalatsa. Chitsanzo: Mfundo zimene ananena zandifika pamtima. Kufika pamtima: Kukhudzika, kukhala ndi chisoni. Chitsanzo: Nkhani imeneyi yandifika pamtima. Kufoila: Kupusa, kulephereka. Chitsanzo: Asiyeni amenewa, ndi ofoila. Kufuna kulowa pansi: Kuchita manyazi kwambiri. Chitsanzo: Atandikalipira pamaso pa anzanga a kusuku- lu, ndimafuna kulowa pansi. Kufuna wopita naye (kufuna wotsagana naye): Ukufuna wakufa naye. Chitsanzo: (1) Samalani ndi mnyamata ameneyu, akungo- funa wopita naye. (2) Samalani ndi mnyamata ameneyu, akungofuna otsagana naye. Kufunga: Kuyanga. Chitsanzo: Maluwa aja anafunga pakhonde ponse. Kufunsa chinyezi kubafa: Kufunsa zomwe ukudziwa kale. Chitsanzo: Zoona n’kumafunsa kuti wakuba amapita naye kuti? Si kufunsa chinyezi kubafa kumeneko! 122