Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 122

Paphata pa Chichewa Kudzukira kumanzere: Kusadzuka bwino. Chitsanzo: Musamuyambe akhoza kukumenyani. Wadzu- kira kumanzere lero. Kufa choimirira: Kumagwirabe ntchito ukudwala. Ndiye anthu akamachenjeza munthu wotero kuti akhoza kufa akugwira ntchito amamuuza mawu amenewa. Chitsanzo: Inutu mudzafa choimirira. Kufa mphuno: Kusamva fungo. Chitsanzo: Mwanayu ndi wakufa mphuno. Kufa mutu: (a) Kusokonekera chifukwa cha chikondi. Chitsanzo: Kodi mwafa naye mutu mnyamata uja eti? (b) Kusaganiza bwino. Chitsanzo: Bambowa ndi akufa mutu. Kufa ndi mseko: Kuseka kwambiri. Chitsanzo: Ukamacheza ndi Mavuto, umafa ndi nseko chifukwa pakamwa pake pamangobulika nthabwala zo- khazokha. Kufa ndi mtima: Kumalakalaka zinthu zomwe sungazipeze. Chitsanzo: Mukuganiza kuti mungagule galimoto, mudzafa ndi mtimatu inu! Kufa nsapato zili kuphazi: Kufa ukugwirabe ntchito mwakhama. Chitsanzo: Wandale uja anafa nsapato zili kuphazi. Kufera fungo: Kulephera kupeza zimene ukufuna. Chitsanzo: Nafenso zabwino timazifuna, koma tikungofera fungo. 121