Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 121
Paphata pa Chichewa
Kudzisinga: Kukhala chete osayankhula kanthu.
Chitsanzo: Ukaona kuti ukhoza kupalamula umafunika
kudzisinga.
Kudzisunga: Kukhala osagonanan ndi munthu mpaka
utalowa m’banja.
Chitsanzo: Anthu amene amadzapeza banja labwino ama-
khala amene ankadzisunga.
Kudzitama: Kunyada, kutumbwa, kuyerekedwa.
Chitsanzo: Munthuyu ndi wodzitama.
Kudzitamandira: Kunena zimene amachita bwino
komanso zomwe ali nazo, kudzitama.
Chitsanzo: Amangokhalira kudzitamandira.
Kudzithandiza: Kuchita chimbudzi, kubiba, kunyera.
Chitsanzo: Koma anthu ndi aluso kwabasi, zoona kud-
zithandiza pakati pansewu ngati pamenepa?
Kudzithangata: Kukabiba, kukanyera.
Chitsanzo: Walowa pachikanga kuti akadzithangate.
Kudzivuta: Kudzivutitsa, kuchita zinthu zomwe
sungapindulepo kanthu.
Chitsanzo: Mwangodzivuta kubwera kuno.
Kudziwonongera: Kudzibibira, kudzinyerera. Angatan-
thauzenso kudzisanzira.
Chitsanzo: Akumangodziwonongera, mwina akudwala
m’mimba.
Kudziyala: Kugona.
Chitsanzo: Ndikatopa ndimangopita kukadziyala.
120