Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 12
Paphata pa Chichewa
Anditembenukira: Andiukira.
Chitsanzo: Mabwenzi anga onse anditembenukira.
Anthanga imodzi: Omwe unabadwa nawo limodzi.
Chitsanzo: Anzanga onse anthanga imodzi anakwatiwa.
Anthu adera: Anthu osawadziwa, anthu omwe si abale
ako.
Chitsanzo: Sindingamathandize anthu adera abale anga
akuvutika.
Anyanya: Awonjeza.
Chitsanzo: Amunanga anyanya nsanje.
Aona mbwadza: Aona zoopsa.
Chitsanzo: Akachita masewera aona mbwadza.
Apo bii: Mawuna amanenedwa pofuna kutanthauza kuti,
ngati zimenezi sizichitika ndichita zakutizakuti.
Chitsanzo: Mubweretse ndalama zanga, apo bii
sindikupatsani katundu wanuyu.
Apo phuluzi: Zikangolephereka zimenezi uona
zakutizakuti.
Chitsanzo: Ubweretse ndalama zanga, apo phuluzi,
ndikupha.
Asukusula:
(a) Achenjera.
Chitsanzo: Tsopano asukusula moti ayamba kutinyoza.
(b) Kutsuka m’maso, kutsuka nkhope ukangodzuka
kumene.
Chitsanzo: Ndipatseni madzi ndisukusule.
11