Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 119
Paphata pa Chichewa
Kudzikhweza: Kudzipha podzimangirira.
Chitsanzo: (1) Alimi ambiri ataona kuti chimanga chawo
chapserera ndi ng’amba, anangodzikhweza n’kufa. (2)
Katundu wawo atapsa ndi moto wolusa, anangodzikhwe-
za.
Kudzikoka: Kuyenda movutikira.
Chitsanzo: Amayenda modzikoka popita kuchipatalako.
Kudzikumbira manda: Kuchita zinthu zomwe zikhoza
kukubweretsera mavuto.
Chitsanzo: Makutu a munthu akangotsekeka, amakhala
kuti wayamba kale kudzikumbira manda.
Kudzikuza: Kuyerekedwa, kunyada.
Chitsanzo: Bambo aja ndi wodzikuza.
Kudziletsa: Kupewa kuchita zinazake zimene umafuna.
Chitsanzo: Munthu wokwatira amafunika kukhala
wodziletsa pochita zinthu zina.
Kudzilimbitsa: Kupirira, kuchita khama kuti usachite zi-
nazake.
Chitsanzo: Ingodzilimbitsani kuti musagone.
Kudziluma: Kulephera kulankhula bwinobwino.
Chitsanzo: Pamene amayankhula amangodziluma.
Kudzimana: Kukhala moyo wovutikirapo mochita
kusankha kuti uchite zinazake zofunika kwambiri. Ku-
khala moyo wovutikirapo zili zoti ukanatha kukhala moyo
wabwino kwambiri.
Chitsanzo: Mkaziyu ndi wodzimana.
Kudzimanga: Kudziletsa kuti usachite chinachake.
Chitsanzo: (1) Thupi lako likayamba kuvuta, umafunika
118