Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 115

Paphata pa Chichewa Kudya ziro: Kulephera zonse. Mawu amenewa amakonda kugwiritsidwa ntchito kusukulu. Chitsanzo: Anzake onse a m’kalasi adya ziro. Kudya: (a) Kulowetsa chakudya m’mimba. Chitsanzo: Ndikudya chimanga. (b) Kukhoza. Chitsanzo: Mwana wanu wadya ziro. Kudyaka: Kuponda. Chitsanzo: Mwana wadyaka nsomali. Kudyakwathu: Zimene timachita, zimene tinazolowera. Chitsanzo: Masewera ampira ndiye kudyakwathu. Kudyana: (a) Anthu oyandikana nyumba onse akakweza kwambiri zoimbira zawo pamalopo n’kumamveka chiphokoso chosamveka bwinobwino. Chitsanzo: Magetsi akangoyaka, anthu a m’nyumba zonse zili apazi amayatsa zoimbira zawo ndipo nyimbo zimadyana. (b) Kuyambana, kukangana. Chitsanzo: Mmene ndimadutsa pamalopo panali pali pokopoko, kaya sadyana kaya. (c) Kugundana. Chitsanzo: Galimoto yawo inadyana ndi galimoto ya apoli- si, moti awatsekera. Kudyeka ndi mafupa omwe: Kugonja kotheratu. Chitsanzo: (1) Sadyeka anadyeka ndi mafuma omwe. (2) Amayerekedwa, lero wadyeka ndi mafupa omwe. 114