Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 114
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Ataona kuti mavuto amupanikiza, anangogani-
za zodya mpamba.
Kudya mtedza waching’onga: Kuiwalaiwala.
Chitsanzo: Mungawauze zinthu n’kumaganiza kuti
azisunga? Anadyatu mtedza waching’onga.
Kudya mtima wa sontho: Kufulumira kuyankhula
kapena kuchita kanthu, kusaugwira mtima, kupupuluma.
Chitsanzo: Mwana wanuyu anadya mtima wa sontho. Sa-
funa nkhani imudutse.
Kudya mutu: Kuganiza kwambiri, kapena kuganizira
nkhani inayake.
Chitsanzo: (a) Ngati ukufuna kupeza yankho lolondola,
uyenera kudya mutu. (b) Usanavomere, umafunika
kuyamba wadya kaye mutu.
Kudya nauzira: Kuyesa kukometsa zinazake n’cholinga
choti upindulepo.
Chitsanzo: Pofuna kuti asasankhe chitenje chabwinocho,
anamulozera china. Amene uja ndi wachinyengo kwambi-
ri, amadya nauzira.
Kudya nthawi: Kugwiritsa ntchito nthawi yopitirira pa
imene unauzidwa, kuwononga nthawi.
Chitsanzo: (1) Zimene mukuchitazi zikungodya nthawi. (2)
Mkuluyutu wadya nthawi.
Kudya wani: Kuchita zakupsa, kukhala patsogolo.
Chitsanzo: Anyamata akuno ndi amene anadya wani
pampikisanowo.
Kudya zankhuli: Kudyera nyama.
Chitsanzo: Ndikufuna kudya zankhuli.
113