Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 113
Paphata pa Chichewa
Kudya kam’lupsa: Kulawa zoipa, kuzolowera zoipa.
Chitsanzo: Mwana ameneyu anaipira kudya kam’lupsa.
Kudya kuwo: Kuchenjeretsa. Mawuwa anabwera poten-
gera zimene zimachitika anthu akamayenda bawo, mun-
thu akamudya mnzake mulu waukulu wa nkhomo.
Chitsanzo: Pamenepa ndiye akudyani kuwotu, kukuten-
gerani mpani ndi mbewa zomwe!
Kudya m’mphunom’mphuno: Kudya mofulumira kwam-
biri komanso kudya zakudya zambiri nthawi imodzi, ena
amati kudya monthunthumira.
Chitsanzo: (a) Osamadya m’mphunom’mphuno ngati
ukuthawa. (b) Anthu omwe amadya m’mphunophuno
amachititsa manyazi.
Kudya milomo: Chichewa chamakono chonena za
kupsopsona munthu kapena kumukisa.
Chitsanzo: (1) Anawapeza akudyana milomo. (2) Ndikufu-
na kudya milomo.
Kudya miseche: Kunena zoipa za munthu wina.
Chitsanzo: Ndikudziwa kuti ndikangochoka muyamba
kundidya miseche.
Kudya moto:
(1) Kukwiya.
Chitsanzo: Atayankhula mawu amwano, mwamuna wake
anadya moto.
(2) Kuchita bwino kwambiri.
Chitsanzo: Gulu la mudzi wathu ndi limene linadya moto
pampikisanowo.
Kudya mpamba: Kuwononga ndalama za bizinezi.
112