Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 11
Paphata pa Chichewa
Anakhala bwanji: Kodi munthu ameneyu ndi wotani?
Chitsanzo: (1) Anakhala bwanji munthu? Ndi wovuta
kumumvetsa, akachita choipa savomera. (2) Kodi mayi
amenewa anakhala bwanji? Zoona osachita manyazi ndi
anthu onsewa!
Anakhulana: Anayambana.
Chitsanzo: Anthuwa akuoneka kuti anakhulana.
Anamuchotsa mbola: Anamuthetsa makani, anafatsa.
Mawuwa anachokera ku zimene njuchi imachita.
Kungoichotsa mbola kapena ikangoluma kamodzi,
imakhala yoti singachitenso kanthu.
Chitsanzo: Masiku ano anafatsako, anzake anamuchotsa
mbola.
Anamulowa mumtima: Anamufika pamtima, anamva
chisoni.
Chitsanzo: Mawu anamuuzawo anamulowa mumtima.
Anamwa tiyi adzamwanso: Zinthu zimasintha, mavuto
amatha.
Chitsanzo: Mukavutika musamataye makapu, anamwa
tiyi adzamwanso.
Anandikhula: Anandimana.
Chitsanzo: Nditawapempha adangondikhula.
Ananditsukuluza: Anandilalatira.
Chitsanzo: Ukanamva chisoni ukanaona mmene
ananditsukuluzira.
Anangoti du: Samayankhula.
Chitsanzo: Mmene timacheza, mnyamatayo anangoti du!
10