Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 108
Paphata pa Chichewa
ntchito m’boma amapita kuntchito kuti akangochongetsa.
Akatero amapachita jekete pampando kuti anthu aziona
kuti abwera, kenako amapita kukayenda ntchuwa.
Kuchotsa akalungusese: Kudyera zankhuli.
Chitsanzo: Tiphe bwampini kuti tichotse akalungusese.
Kuchotsa mimba: Kupha mwana wosabadwa.
Chitsanzo: Mtsikanayu wachotsa mimba.
Kuchotsa mimba: Kupha mwana yemwe sanabadwe.
Chitsanzo: Azimayi ambiri amapita kuchipatala kuti
akachotse mimba.
Kuchotsa pakati: Kupha mwana wosabadwa.
Chitsanzo: Mtsikanayu wachotsa pakati.
Kuchotsa pathupi: Kupha mwana wosabadwa.
Chitsanzo: Mtsikanayu wachotsa pathupi.
Kuda m’kamwa: Kutukwana.
Chitsanzo: Makolo ake ndi akuda mkamwa.
Kuda m’manja: Kusauka kwambiri.
Chitsanzo: (a) Kadziotche wakeyo ndi ndani yemwe akufu-
na kukwatiwa ndi kada m’manja ngati amene uja. (b)
Ukada m’manja usaloze zala anzako omwe
zikuwayendera.
Kuda nkhawa: Kusowa mtendere mumtima chifukwa cha
zimene zachitika, zimene ukukumana nazo kapena
zimene ukuyembekezera.
Chitsanzo: Kuda nkhawa kumayambitsa matenda. (2)
Osamada nkhawa ndi zimene sizinachitike, mwina siz-
ichitika mkomwe!
107