Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 107
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Munthu ameneyu amachita bwino mump-
ingo. (2) Munthuyu amachita bwino zinthu.
Kuchita dzanzi:
(a) Kuzizira kapena kusiya kumva thupi likagwiridwa.
Chitsanzo: Mwendo wanga wachita dzanzi.
(b) Zochititsa mantha.
Chitsanzo: Zimene wachita ndi zochititsa dzanzi.
Kuchita nacho: Kudya kapena kumwa.
Chitsanzo: Koma alendo aja ndiye achita nayotu nsimayi!
Kuchita zazikulu: Kuchita zinthu zolongosoka.
Chitsanzo: Akulimbikira maphunziro kuti adzachite
zazikulu m’tsogolo.
Kuchita zithu mowawanya: Kuchita zinthu mosa-
longosoka.
Chitsanzo: Anthuwa akuchita zinthu mongowawanya.
Kuchita zoopsa: Kukhaulitsa.
Chitsanzo: Anamuopseza kuti akadzabweranso
adzamuchita zoopsa.
Kuchita zopusa: Kugonana.
Chitsanzo: Anawapezerera akuchita zopusa.
Kuchoka mano: Kutha ntchito, kutsika paudindo, ku-
lephera kuchita chinachake.
Chitsanzo: (1) Ife tinachoka mano, sitingakwanitse kuchita
zimenezi. (2) Likanakhala kale tikanakwanitsa, koma pano
tinachoka mano.
Kuchongetsa: Kungopitako kuti aone kuti wafika.
Chitsanzo: (1) Ndipitako kuti ndikangochongetsa, aka-
kandiona ndizikabwerako. (2) Anthu ambiri ogwira
106