Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 104
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Tamubwanyuleni pakamwa watukwanayo!
Kubwebwetuka: Kuyankhula mosaganiza, kulongolola.
Chitsanzo: (1) Udzayerekeze kubwebwetuka pali ine, ndi-
dzakubwanyula pakamwa. (2) Amakonda kubwebwetuka
akaona anthu.
Kubwekera: Kuyamikira kukoma kwa chinthu.
Chitsanzo: Alendowa akungobwekera chilichonse.
Kubwenje: Kudzenje, kuphanga.
Chitsanzo: Ndalama yake yagwera kubwenje.
Kubwerera kukhosi: Kufunsa kusanza, kukanika ku-
meza.
Chitsanzo: Chakudyachi chikundibwerera kukhosi.
Kubwerera m’mbuyo: Kusiya kuchita bwino, kufooka,
kulephera.
Chitsanzo: (1) Abusawa ndi amene akuchititsa kuti
Akhristu ambiri abwerere m’mbuyo. (2) Poyamba
ankakhoza bwino m’kalasi, koma pano wabwerera
m’mbuyo.
Kubweza moto:
(a) Kubweza mwano.
Chitsanzo: Mwanayu wayamba kudziona kuti wakula moti
akumabweza moto.
(b) Kuugwira mtima, kuchepetsa nkwiyo.
Chitsanzo: Anabweza moto anzawowo atawapepesa.
Kubwibwitsa: Kuyankhula mwachibwibwi.
Chitsanzo: Amati akakwiya amayamba kubwibwitsa, ke-
nako amangowapulumutsa makofi.
103