Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 101
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Nyimbo imeneyi imandibanda.
Kubandulana: Kumenyana.
Chitsanzo: Ana amadererana ajatu abandulana lero.
Kubaya mumtima: Kupweteka mumtima.
Chitsanzo: Zimene anena zandibaya mumtima.
Kubaya suti: Kuvala suti.
Chitsanzo: Adutsa pompa atabaya suti yawo.
Kubenthulako:
(a) Kunenako pang’ono.
Chitsanzo: Bwerani ndikubenthulireni zimene ananena.
(b) Kuswa, kugamphula chinthu.
Chitsanzo: Ndani wabenthula khaka langa?
Kubereka kopenyetsa kamtengo: Kubereka kwambiri.
Chitsanzo: Anthu akuberekana kwambiri m’dzikoli, moti
kuberekana kwake ndi kopenyetsa kamtengo. Nanga dziko
ling’onong’onoli!
Kubetcha: Kupereka chinachake monga chitsimikizo
choti zimene ukunenazo zichitikadi.
Chitsanzo: Anthu onse abetcha ndalama ndipo akuti timu
imeneyi ipambana.
Kubetsa: Kuluza, kusaganiza bwino, kutaya.
Chitsanzo: (1) Kukwatira ndi amene uja ndi kubetsa. (2)
Koma ndiye mwabetsatu, kugulitsa nsalu 100 kwacha!
Kubinya: Kuvulala pamalo olumikizira mafupa.
Chitsanzo: Akuyenda pintchapintcha chifukwa wabinya.
Kubisala pachipande: Kunama.
Chitsanzo: Mwabisalatu pachipande, nsana ukuonekera.
100