Paphata pa Chichewa
Ana akumpanda: Ana a mabwana, ana okula moyo
wofewa.
Chitsanzo: Usadzayerekeze kufunsira mwana
wakumpanda.
Ana akumpani: Mbewa.
Chitsanzo: Munthu wamtundu wanji wobadwira ku Mala-
wi kuno koma osadziwa ana a kumpani!
Ana ndi chuma: Mawuwa amatanthauza kuti tsogolo la
dziko limadalira ana.
Chitsanzo: Anthu ambiri anayamba kubereka ana
ochuluka poganiza kuti ana ndi chuma.
Ana ofewa: Ana onjoya, osangalala ndi moyo.
Chitsanzo: Ife ndi ana ofewa, sitidandaula ndi zambiri.
Anabwereketsa makutu: Ndi wosamva.
Chitsanzo: Achimwene anuwa anabwereketsa makutu.
Anafa mutu:
(a) Saganiza.
Chitsanzo: Anzanuwa anafa mutu, sangakuthandizeni
mutawafunsa maganizo.
(b) Kutengeka ndi mnyamata kapena mtsikana mpaka
kufika posokonezeka.
Chitsanzo: Zimene umachita zija zimasonyeza kuti unafa
naye mutu mtsikana uja.
Anagonerapo onsewa: Mawuwa amanenedwa posonyeza
kuti munthu wina ankangokhulupirira aliyense,
anakhulupirirapo onsewa.
Chitsanzo: Mnyamata uyu anagonerapo onsewa.
9