Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale | Page 50

Ngale Mtima wa Kino unasungunukiratu atawona malodzawa. Moto unali ukuthamuka ndi ukali ndipo kuwala kwake kunkawunikira ponsepo. Kuwalako kunamupatsa Kino mantha aakulu, makamakanso atakumbu- kira munthu anamupha uja. Nthawi yomweyo anagwira dzanja la Juana n’kuthawira pamalo ena obisika. Kenako anayenda mumdima n’ku- malowera kunyumba kwa Juan Tomas ndipo atafika anangolowa m’nyumba kuti tswere. Atalowa anangokhumata chapakona. Iwo ankatha kuwona kuwala kwa moto uja kudzera pamipata ya nyumbayo. Kenako anamva denga likuloshokera mkati ndipo motowo unadya mitengo komanso udzu wonse n’kutsala phulusa lokhalokha. Posakhalitsa anayamba kumva kulira kwa azinzake. Anamvanso mlamu wake uja, Apolonia, akulira kowopsa. Iye ndi amene anali wachibale wapafupi yekhayo yemwe anali kumene kunkayaka motoko, choncho ankalira kwambiri kuposa azimayi ena omwe ankaganiza kuti Kino ndi Juana apsera m’nyumbamo. Kenako Apolonia anathamangira kunyumba kwake. Atangofika, Ki- no anamuyankhula chapansipansi, “Apolonia, usalire. Tili moyo. Tapita ukayitane mwamuna wako. Chonde usawuze munthu winanso chifu- kwa miyoyo yathu ikhala pangozi.” Patangotha mphindi zochepa, Juan Tomas anatulukira ndipo cha- pansipansi anawuza mkazi wakeyo kuti: “Apolonia, uwonetsetse kuti aliyense asalowe muno.” Kenako anatembenukira kwa Kino n’kunena kuti, “Chachitika n’chiyani m’bale wanga?” “Munthu wina amafuna kundichita chipongwe,” anatero Kino. “Ndiye pamene ndimalimbana naye ndinamupha.” “Ndi ndani?” anafunsa Juan Tomas mofulumira. “Sindikudziwa. Kunali chimdima moti palibe chimene ndinawona.” “Ndi ngale ija ndithu,” anatero Juan Tomas. “Ngale ija ndi yoyipa Kino.” “Nditachoka pamenepo ndinapita kudoko kuti ndikakankhe bwato lathu kuti tithawe. Koma ndapeza kuti labowoledwa. Kenako ndinagani- za zoti ndidzawuze mkazi wanga, koma pamene ndimafika kuno nda- peza nyumba yathu ikunyeka. Panopa tilibenso kothawira. Chonde 44