Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale | Page 44

Ngale wina. Juana anaponya pansi fuwa lija ndipo anapita pamene panali mwamuna wakeyo n’kukamudzutsa. Kenako anayenda naye mpaka m’nyumba. Magazi ankatsetsereka pachipumi chake chija, chomwe tsopano chinali chitasendeka kwambiri. Chifukwa cha kukula kwa nde- wuyo, zovala zake zinali zitatheratu moti malaya ake anali nsanza zo- khazokha. Nalonso buluku lake linali litangotsala pang’ono kuvuka. Ki- no anakokera bulukulo ndipo Juana anamuthandiza kukhala pansi. Jua- na anali mkazi wapadera, mwinanso tinene kuti anali chozizwitsa kwa Kino, koma kungoti Kino sankadziwa. Mwina akanadziwa zimenezi si bwenzi akulimbana ndi ngaleyi. Tikutero chifukwa atawona magazi akuyenderera pachipumi cha mwamuna wakeyo, Juana anakokera siketi yake n’kuyipinda kumapeto. Kenako anayamba kupukuta chipumi cha mwamuna wakeyo mwachikondi pogwiritsa ntchito siketiyo. Akanakha- la wina, bwenzi atamutsira mphepo chifukwa vutoli linabwera chifukwa cha kusamva kwake. Atamaliza kumupukutako, Juana anapita kukamu- tungira madzi akumwa. Kino anamwa madziwo n’kuyamba kupukusa mutu wake kuti nthangala ya ubongo wake ibwerere pachimake. “Ndi ndani?” anafunsa Juana. “Sindikudziwa,” anatero Kino. “Sindinamuyang’ane nkhope.” Atawona kuti magazi akutulukabe ambiri, Juana anapita kukatenga poto wamadzi ndi nsanza n’kuyambanso kusunsa magazi pachipumi cha mwamuna wakeyo. Pa nthawiyi chikumbumtima chinamulasa Kino moti ankafuna kulira. “Kino mwamuna wanga,” anatero Juana, koma mwamuna wakeyo anayang’ana kumbali kuti mkazi wakeyo asawone misozi yomwe in- alengeza m’maso mwake. “Mwamuna wanga chonde, tiye titaye ngaleyi. Ngaleyi ndi yoyipa, ikhoza kuwononga banja lathu. Tiye tiyiphwanye ndi mwala. Kapena tikangoyitaya m’nyanja momwe inachokera. Bambo a Coyo, ngaleyitu ikhoza kubweretsera masoka!” Pamene ankayankhula mawu amenewa, maso a Kino anayambanso kuwala. “Ayi,” anatero Kino. “Ndimenya nkhondo imeneyi mpaka pama - 38