Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale | Page 43

Ngale wanga.” Juan Tomas anasasa matako ake n’kuwona nsanawanjira. M’mbuyo muno, Kino anakhala pansi n’kumasinkhasinkha. Maganizo omwe anali nawo anamufowola kwambiri ndipo ankangodziwona ngati akulimbiki- ra mtunda wopanda madzi. Zinkangokhala ngati njira zonse zomwe amafuna kudutsa zatsekeka. M’mutu mwake ankangomva nyimbo yamdima wandiweyani. Juana atayang’ana mwamuna wakeyo n’kuwona mmene anawerami- ra ndi nkhawa, nayenso anayamba kuvutika mumtima. Koma Juana ankamudziwa bwino mwamuna wakeyu. Iye ankadziwa kuti ngati pali chomwe angachite kuti amutonthoze komanso kumulimbikitsa pa nthawi yovutayi, ndiye ndi kungokhala chete basi. Kenako anayamba kuyimbira nyimbo mwana wake yemwe anali m’manja. Iye ankayimba nyimboyi ngati njira yotonthozera mwanayo komanso kuthamangitsa zoyipa. Mawu amene ankawaluka m’nyimboyi anali anzeru kwambiri chifukwa ankadziwa kuti agweranso m’makutu a mwamuna wakeyo. Kino sanasunthe pamene anakhala paja kapena kufunsa za chaku- dya chake. Iye ankatha kuwona mikwingwirima yomwe ankayembeke- zera kukumana nayo. Ankadziwa kuti pali achiwembu ambirimbiri om- we ankalakalaka atatuluka panja mumdimawo kuti akamuchite chipo- ngwe. Mwamwayi, Kino sankayerekeza kuchoka panyumba pake. Koma ngati pali chinthu chovuta kwambiri komanso chosathawika ndiye ndi mavuto. Akawona kuti sukumadutsadutsa pakhomo pawo, mavutowo amakuyendera kwanu. Ndi zimene zinachitika patsikuli. Mwadzidzidzi, Kino anamva munthu wina akumuyitana. Atangomva kuyitanako, anatenga mpeni wake n’kuyamba kutuluka panja kuti akawone kuti ndi ndani. Juana anayesetsa kumuletsa kuti asatuluke, koma Kino anatseka ma- pirikaniro ake. Juana anamutsatira n’kumugwira nkono, koma Kino ana- wusasa n’kulowa mumdima. Posakhalitsa Juana anamva anthu akumenyana modetsa nkhawa. Mwamantha anayika pansi mwana wake n’kutola fuwa ndipo anathamangira panja paja, koma anakapeza nde- wuyo itatha kale. Kino anali ali m’dothi, kwinaku akuyesetsa kudzitolera kuti adzukenso. Chodabwitsa n’choti panjapo panalibenso munthu 37