Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale | Page 16

Ngale wake. Wantchito uja anagogoda chitseko n’kumadikira kuti awuzidwe zoti alowe. “Eya?” anatero dokotalayo. “Kwabwera Mwindiya wina panjapa. Akuti mwana wake walumid- wa ndi pheterere.” Dokotalayo anayika pansi kapu yake modekha mkwiyo ukusonkha- na pankhope yake. “Koma mutu wako umagwira? Ukuganiza kuti ndikusowa chochita kuti mpaka ndiyambe kuthandiza ana a anthu osasamba omwe alumid- wa ndi apheterere? Inetu si dokotala waziweto!” “Chabwino bwana,” anatero wantchitoyo. “Kapenatu wakuwuza kuti ali ndi ndalama?” anafunsa dokotala uja. “Ngati ali wamatumba obowoka umuwuze kuti akagwere uko. Ine sindinabwere kuno kudzagwira ntchito zachifundo. Ndinabwera kudza- panga ndalama. Ndatopa kuthandiza anthu awulesi omwe amangofuna chithandizo chawulere. Pita ukamufunse kaye ngati wabwera ndi chilembwe!” Atafika pageti, wantchitoyo anatsegulanso geti lija pang’ono n’kuyang’ana anthu anali panja aja. Ulendo uno anayankhula m’chinenero chotsalira chija. “Kodi muli ndi ndalama yoti mulipire?” Kino anachotsa bulangete anafunda lija n’kupisa m’thumba ndipo anatulutsa kapepala kapusitiki komwe anakapinda mawulendo ambi- rimbiri. Kenako anayamba kutambasura pepalalo kuti wantchito uja awone tingale tokwana 8 timene anali nato. Tingaleto tinali tonyansa ngati ndowe za mbuzi, moti kwa ena tinali topandiratu ntchito. Wa- ntchitoyo analandira kapepalako n’kutsekanso geti. Ulendo uno sa- nachedwe kubwera ndipo anatsegulanso getilo n’kupereka ndowe zija kwa Kino. “Dokotala wachokapo,” anatero wantchitoyo. “Kunabwera anthu ena kudzamutenga kuti apite kukathandiza wodwala wina kumtun- daku.” Atatero anatsekanso geti mwamphamvu n’kumusiya Kino ndevu 10