Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale 2 | Page 67

Ngale yo inkangokhala ngati chinthu chowola m’maso mwake. Kenako anate- mbenukira kwa mkazi wake kuti amupatse ngaleyo. Pa nthawiyi Juana anali atagwira nsalu yomwe anakulungamo chinthu chamagazi chija. Atangowona ngaleyo, misozi inalengeza m’maso mwake ndipo anawuza mwamuna wakeyo kuti, “Ayi, itayeni inuyo.” Kino anasonkhanitsa mphamvu zake zonse n’kuvungira ngaleyo m’nyanja. Anthu onse anayiperekeza ndi maso pamene inkawuluka m’malere, ikuwala ndi dzuwa lamadzulowo. Kenako inagwera m’madzi n’kulowa pansi pa nyanja. Kino ndi mkazi wake anayima kwa kanthawi asakukhulupirira kuti alekana ndi chinthu chomwe chinkawabweretsera mavuto. Pansi pa nyanjayo, nkhanu ina yongodziyendera inaponda mo- sasamala n’kuvundula matope omwe anakwirira ngale ija. Kungocho- kera tsiku limenelo, nyimbo ya ngale sinamvekenso m’mutu mwa Kino. 61