Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Ngale 2 | Page 31

Ngale Koma Kino sanasiye kuyang’ana kabotolo kamankhwala oyera aja. Ankayang’ana botololo tsinya lili the-e! Posakhalitsa Coyotito anasiya kulira ndipo anagona tulo chifukwa chotopa ndi kulira komanso kusan- za. Kenako dokotayayo anapereka Coyotito kwa mayi ake. “Apeza bwino tsopano,” anatero dokotalayo. “Ndachotsa poyizoni yense yemwe anatsalira m’thupi mwake.” Juana ankayang’ana doko- talayo momuyamikira. Dokotalayo anatseka chikwama chake n’kunena kuti, “Mukuganiza kuti mupereka liti ndalama ya chithandizo chamankhwala chomwe nda- perekachi?” Dokotalayo ananena mawu amenewa mwawulemu kwam- biri. “Tikupatsani tikangogulitsa ngale yathu,” anatero Kino. “Kodi muli ndi ngale? Sindimadziwatu ine!” dokotalayo anafunsa mwachidwi. Kenako anthu oyandikira nyumba aja anayamba kunena mokweza kuti, “Wapeza ngale yamtengo wapatali kwambiri.” Ankanena zimenezi akuyerekezera kukula kwake ndi zala zawo. “Kino alemera ndithu,” anatero anthuwo. “Palibe anayamba wawonapo ngale yokongola ngati imene Kino wapeza.” Dokotalayo anayamba kuyang’ana mwawusatana. “Koma uku- mayisunga pabwino ngaleyo? Ukapusatu anthu akuwomba. Bwanji ndizikakusungira kunyumba kwanga pamalo abwino?” “Musavutike, ndikumayisunga pabwino,” anatero Kino. “Mawa ndi- kayingulitsa ndipo ndibwera kudzakupatsani ndalama yanu.” Maso a dokotalayo anatsata maso a Kino pamene ankayenda molowera pansi, chakukona kwa nyumba yakeyo. Chule anadabwa m’madzi muli mwake. Kino atawona mmene maso a dokotalayo anayendera, anazindikira kuti pali kanthu. Dokotalayo ko- manso anthu aja atangochoka, Kino anatseka chitseko n’kupita pamene anakwirira ngale ija. Kenako anayifukulapo n’kukayikwirira pansi pa phasa yomwe ankagonera. Juana ankangomuyang’ana modabwa. 25