Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 98

Miyambi ya Patsokwe Kumana anzako n’kudzimana wekha. -Ukathandiza mnzako umakhala ngati wadzala, mawa adzakuthandiza iweyo. Kumana n’kubisa. -Si bwino kumanamiza ena. Kumana n’kudzipha. -Ukathandiza mnzako umakhala ngati wadzala, mawa adzakuthandiza iweyo. Kumanda kulibe chisoni. -Kumanda kumatenga aliyense, kaya ndi mphawi, wamkulu kapena amene sanalidyerere dzikoli. Kumanda kumapita anthuanthu, n’kusiya zitsiru. -Anthu abwino sakhalitsa padzikoli. Kumanda sankira dumbo. -Mawuwa amatanthauza kuti tikakhala pamavuto tisamaloze ena chala kuti ndi amene akuchititsa. Kumanda sikupita mtolo wa udzu, kumapita mtembo wa mun- thu. -Kaya munthu amachita zabwino chotani, tsiku lina adzamwali- ra n’kupita kunsabwerera. Kumanga khobwe ndi m’mawa. -Pofuna kuchita zinthu ndi bwino kuzichita mopanda chidodo kapena mosachedwa. Kumanga mlaza m’maso. -Pofuna kukwatira pamafunika kulimba mtima. Umafunika ku- khala ngati wamanga nsalu m’maso kuti usachita manyazi. Kumanga mwamanga, koma anyamkalere. -Anyamkalere ndi timaulusi tomwe timangoti balalabalala mun- thu akamanga zinazake. Tiyenera kuonetsetsa kuti chilichonse 97