Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 97

Miyambi ya Patsokwe zosakhala zenizeni. Kulinda mdima ndi nthanthi zako. -Nthanthi ndi nkhani kapena nthano. Mawuwa amanena za munthu amene akungonena nkhani mozungulira mpaka mdima kugwa. Tikamanena zinthu ndi bwino tizipewa kunena nkhani mozungulira. Ndi bwino kumangotumbula. Kulinji akudza ndi njira. -Tikamakhala tizikonzekera chilichonse. Zinthu zimatha kusin- tha mwadzidzidzi. Kulirira kuutsi. -Mawuwa amanenedwa ngati wina wakumana ndi mavuto chifukwa chosamva ndiye akuyesa kuphumba anthu m’maso kuti asadziwe kuti akuvutika chifukwa cha kusamvako. Ama- khala ngati wakhala pamene pali utsi kuti anthu aziti akulira ndi utsiwo, chonsecho akulira chifukwa cha ululu. Kuliza ng’oma yowambawamba. -Mawuwa amanenedwa ngati wina wachita zimene ena ama- yembekezera. Kapena ngati wachita zinthu zimene enanso ama- funa. Mwachitsanzo, mkazi amene wafunsiridwa zili zoti nayen- so amamufuna angavomere poyankha mwamanyazi kuti, “Mwayimba ng’oma yowambawamba.” Kuloza ndi chala. -Mawuwa amanenedwa ngati munthu wina anachita zinthu zomwe zamubweretsera mavuto monga kuba kapena kuchita mwano. Kulumpha dzenje n’kulionera patali. -Vuto silivuta kuthana nalo ngati walionera patali. Ndi bwino kumakonzekera tisanakumane ndi mavuto. 96