Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 96

Miyambi ya Patsokwe Kulaula n’kuzula m’mera. -Mawuwa amanenedwa munthu akayankhula mosabisa mawu kapena kuti mwatchutchutchu. Kulawa kumatha mphika. -Osamakhala munthu wokomedwa ndi zinthu chifukwa ukhoza kukumana ndi mavuto. Kulemera ndi kudya, ukavala malaya akubera. -Palibe amene angakulande chimene wadya, choncho kulemera ndi mmene umadyera osati zinthu zimene anthu ena akhoza ku- kubera n’kukhala zawo. Kulemera ndi kudya. -Kudya bwino n’kumene kungasonyezedi kuti munthu ndi wolemera. Palibe amene adzalowe m’manda ndi katundu. Aku- ba akhoza kukubera katundu wako koma sangakubere chimene chalowa m’mimba. Kuli zii, azimu adutsa. -Anthu akangoti zii amati azimu adutsa chifukwa safuna phoko- so. Mawuwa anayamba chifukwa cha zikhulupiriro zoti kunja kuno kuli mizimu. Kulibe manda a mbeta. -Aliyense amakaikidwa kumanda akamwalira. Choncho, tisamade nkhawa ena akamatinena kuti timwalira tisanakwa- tiwe kapena kukwatira. Kulimana pamsana. -Mawuwa amatanthauza kuchenjeretsana. Akakhala kuti amene wachenjeretsedwa ndi mmodzi, amati amulima pamsana. Kulimbikira mtunda wopanda madzi. -Mawuwa amatanthauza kulimbikira kuchita zinthu zomwe sungaphulepo kanthu. Angatanthauzenso kuwerengera zinthu 95