Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 95

Miyambi ya Patsokwe akamuthamangitsa uku amapita kwinako. Koma banja loteroro limakhalanso ndi mavuto osaneneke monga nsanje komanso kusasonyezedwa chikondi chokwanira. Kukwatira mkazi wokongoka n’chimodzimodzi kudzala mtengo wamango m’mbali mwa njira. -Mavuto amene wakwatira mkazi wokongola ndi munthu ame- ne wadzala mtengo wamango m’mbali mwa njira, amafanana chinthu chimodzi: Onse amavutika ndi anthu akuba! Kukweza bankha patsekera. -Munthu sungakweze bankha patsekera, likhoza kuthyoka. Munthu wamkulu asamachite zibwana kapena kumasewera ndi ana. Kulamula Vumbwe n’kulinga uli ndi Nkhukhu. -Munthu usamapalamule kapena kuputa dala mavuto ulibe pothawira. Kuti ulamulire anthu umayenera kukhala ndi ndala- ma kapena mphamvu. Kulanda mwana n’kudyetsa. -Munthu ungathe kutenga ndi kulera mwana ngati un- gakwanitse kumudyetsa bwino. Kulanga nyani n’kuphwanya mutu. -Poweruza mlandu, si bwino kumawiringula. Umafunika kunena cholakwa chenicheni chimene munthu wachita. Ukatero zimakuyendera. Kulasa mtengo n’chamuna chomwe. -Mlenje wina anaphonya Njati n’kukhapa mtengo. Ngakhale anaphonya, komabe anachita chamuna ndithu. Ndi bwino kuti nafenso tiziyesetsa kuchita khama pochita zinthu, zizichita kukanika zokha. 94