Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 94

Miyambi ya Patsokwe sanaitanidwe angatsatire, choncho woitanayo amanena kuti, “Ndakhululukira mamina a fodya.” Mwambiwu ungatan- thauzenso kuti kanthu kakang’ono kakhoza kubweretsa mavuto aakulu. Kukoma kwa dziko n’kulinga utakhalako. -Kukhala ndi umboni weniweni wa chinthu n’kulinga utachiona komanso kukhala nacho. Kukoma kwa mnzako ndi kamba wako. -Kuti munthu udziwe khalidwe la munthu, umafunika kungo- yang’ana amene amacheza nawo. Munthu ukhoza kuweruzidwa chifukwa cha khalidwe la anzako. Mbiri yako ikhoza kuipa kapena kukoma chifukwa cha amene umayenda nawo. Kukoma ndi kuwonjezera. -Zinthu zimakongola kapena kukhala bwino kwambiri ukamazikongoletsa kapena kuziwonjezera. Kukondwa ndi kuonetsa mano. -Kusangalala kwenikweni kumaoneka. Pali ena omwe amasek- erera n’kumaoneka ngati adya tsabola. Kukula mphuno sikudziwa kumina. -Kuchenjeretsa sikusonyeza kuti munthu amadziwa zonse. Kukula mutu si nzeru. -Nzeru zenizeni zimaoneka ndi zosankha za munthu, osati chifukwa choti anabadwa kale kapena ndi wamkulu mutu. Kukula saimbira maseche. -Munthu asamadikire kuti ena achite kumuuza kuti wakula. Ayenera kusintha yekha n’kumachita zinthu ngati wamkulu. Kukwatira chiwiri kudakoma. -Chinthu chilichonse chili ndi poipira ndi pabwino pake. Mwachitsanzo, munthu amene wakwatira chiwiri, amati 93