Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 93

Miyambi ya Patsokwe kuti wachita bwino. Iye angayankhe modzichepetsa kuti, “Kukana nsalu ya akulu n’kuviika.” Akuluakulu akatituma, si bwino kukana koma kungochita zomwe tingathe. Kukankha konjuta. -Mawuwa amanena za munthu amene akupereka chifukwa chosamveka bwino chomwe walepherera kuchita zinazake. Kukhala awiri si mantha. -Anthu akakhala awiri amatha kuchita zinthu modalirana ndipo amatha kuthandizana wina akapeza mavuto. Kukhala kumunda n’kuona ndime. -Osamangodzichemerera ndi pakamwa pokha, koma anthu aziona ntchito za manja athu. Kukhala kwa eni n’kuomba m’manja. -Munthu ukakhala kwa eni umayenera kumalemekeza anthu amene wawapeza. Kukhala kwa eni ndi kuweteka. -Munthu ukakhala kwa eni umayenera kufatsa. Ukamachita matukutuku amakuthamangitsa. Kukhala m’chiluli n’kuyambirira. -Mawu akuti kukhala m’chiluli akutanthauza kukhala ndi zo- chuluka. Tisamazengereze tikafuna kuchita kanthu. Tisamachedwe pochita zinthu. Kukhala owolowa manja n’kulinga uli ndi kanthu. -Munthu yemwe alibe kalikonse sangagawire ena zinthu, nanga azitenga kuti? Kukhululukira mamina a fodya. -Anthu amene amafwenkha fodya, amatha kufwenkhera limodzi ndi mamina n’kuwakhululukira chifukwa cha fodyayo. Pamene munthu waitana munthu m’modzi yekha, ambiri amene 92