Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 91

Miyambi ya Patsokwe popeza zamawa sizidziwika, ndi nzeru kumasunga zoti zidza- tithandize pamavuto. Kufuna Lumbe chifukwa cha mthenga, koma osadya nyama yake. -Anthu ena amakukonda chifukwa cha zabwino zimene uli nazo, zikatha amakuthawa. Kufunsa ndi kudziwa njira. -Ngati sukudziwa zinazake, m’malo mongozichita, ndi bwino kufunsa kaye kuti uzichite bwino. Kugona m’kuka n’chitatu. -Mwambiwu umanena kuti kugona m’kuka, kapena kuti nyum- ba ya mayi ako, ndi uchitsiru wotheratu. Munthu akakula ama- funika kudziimira payekha. Choncho, si bwino kumadalira ma- kolo nthawi zonse kuti atithandize. Kugona pakati n’kuyambirira. -Kuti munthu upeze malo abwino pagulu, kaya ukukagona ku- maliro, umayenera kufulumira kwambiri. Ndi bwino kumachita zinthu moyambirira ngati ukufuna zikuyendere bwino. Pofuna kuchita zinthu ndi bwino kuzichita mosachedwa. Kugonagona kumapangitsa tsitsi kufula. -Mawuwa amatanthauza kuti kukhala ndi moyo, kapena kuti kugona masiku ambiri, kumachititsa tsitsi liyere kapena kuti ukalambe. Akuluakulu ndi amene amadziwa bwino zapadzikoli. Choncho, ndi bwino kumawafunsa malangizo pa nkhani zosi- yanasiyana. Kuika mkute n’kupangana. -Munthu akamachita zinthu ndi ena, ndi bwino kumayamba mwapangana, osamangochita zokomera munthu mmodzi. 90