Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 88

Miyambi ya Patsokwe Kudandaula sikuthetsa m’landu koma kuyankhulapo. -M’malo momangodandaula ndi bwino kuchita khama kuti vuto lathulo lithe. Kudandaula sikuthetsa njala koma kusunja. -M’malo momangodandaula ndi bwino kuchita khama kuti vuto lathulo lithe. Kusunja ndi kupempha kwa ena kuti akuthandize. Kudumpha dzenje n’kulionera patali. -Ukadziwa vuto ukhoza kupeza njira yolipewera. Kudya kudamanitsa vimvi mapiko. -Tisamachedwe kuchita zinthu zimene zingadzatithandize m’tsogolo. Vimvi inachedwa kupita kokalandira mapito chifu- kwa cha kudya. Pamene imapitako inapeza mapiko atatha. Kudya kwa mnzako sungamwere madzi. -Munthu azidzidalira yekha pogwira ntchito m’malo modalira ena. Sungamawerengere kuti chifukwa choti wina wadya ndiye kuti iwe umwera madzi, madziwo akapeza chiyani m’mimbamo popeza amadya ndi mnzako! Nafenso tisamadalire kuti ena ag- wire ntchito kuti atithandize, tizichita khama. Kudya lapi, kulima kwete. -Pali anthu ena omwe amasangalala pakudya, koma akauzidwa kuti agwire ntchito amakana kapena amanamizira kudwala. Munthu amayenera kudya thukuta lake. Kuti munthu apeze chinthu amayenera kuchivutikira. Ena kuwauza kuti, “Iwe tiye kumunda,” amayankha kuti, “Ndikudwala ineeeeee!” Koma ku- wauza kuti, “Tiye kumowa,” uwamva akuyankha kuti, “Bola ndikhoza kudzikoka.” Kudya n’kudya, umakumbuka polowa. -Tikakhala pabwino tisamaiwale kumane tachokera kapena mavuto omwe takhala tikukumana nawo. 87