Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 86
Miyambi ya Patsokwe
Tisamangodikira kuti ena azitithandiza ifeyo n’kumangokhala
phwi osawathandiza. Zikatero nawoso amatopa n’kusiya
kutithandiza.
Konza kapansi kuti kam’mwamba katsike.
-Ngati ukufuna kulandira zabwino kuchokera kwa anthu enaake
umayenera kuonetsa khalidwe labwino kuti anthuwo akopeke.
Munthu ukafuna kuti anthu akuchitire chabwino, umafunika
kuyamba ndiweyo kuwachitira zabwino.
Kopanda ntchito umataya.
-Chilichonse ndi chaphindu panthawi yake.
Koyenda sawononga pakumwa.
-Munthu ukakhala kwanu si bwino kumachitira alendo mwano.
Kubala kwa chule ndi kwa thesi n’kumodzi.
-Mawuwa amatanthauza kuti onse ndi anthu ngakhale atakhala
kuti ndi osiyana khungu, chikhalidwe, msinkhu, kukongola ndi
zina zotero.
Kuchedwa kumphero mseche uchuluke.
-Mawuwa amanenedwa akaona kuti azimayi akuchedwa
kubwera kuchokera kumadzi kapena kuntchini. Amaona kuti
kumeneko amachedwa ndi kunena miseche.
Kuchenjera kwa Kalulu kunaphetsa Ankhwere.
-Pali anthu ena odziwa kuzunguza lirime kwambiri, omwe
amatha kuika anzawo m’mavuto ndi zonena zawo. Tiyenera ku-
chenjera ndi anthu oterewa.
Kuchenjera kwa Nkhandwe, kolangiza ena kuti adule michira
chifukwa wake waduka.
-Osamapusitsa ena n’cholinga choti nawonso agwere m’mavuto,
kapena kuti mufanane.
85