Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 85

Miyambi ya Patsokwe Khotekhote ngwa njoka, umatsata kwaloza mutu. -Pofuna kumvetsa nkhani ndi bwino kupeza mutu wa nkhaniyo. Khotekhote ngwanjira, palinga mtima mpomwepo. -Ngakhale njira yopezera chinthu itakhala yaitali, ngati munthu waikapo mtima umachipeza. Khoza limapita ndi mwini dzanja. -Sungakakamize munthu kuchita zimene sakufuna. Khwangwala wamantha adafa ndi ukalamba. -Munthu akasamalira moyo wake amakhala ndi moyo wautali. Koma tambwali amafa nthawi yake isanakwane. Munthu wamantha amakhala zaka zambiri ndi moyo chifukwa man- thawo amamuthandiza kuti asamachite mphulupulu zomwe zingachititse kuti afe msanga. Kodi kuimirira kwakupindulitsa chiyani, anzako akupindula ndi werawera? -Tizigwira ntchito molimbika kuti tipeze zosowa zathu. Polima timawerama osati kuimirira. Kodi mtengo wopanda tsinde mudauona? -Chilichonse chimakhala ndi poyambira pake. Komekome ngwa m’kamwa, kampeni kali pafunkha. -Pali anthu ena omwe amasangalala ndi anzawo pakamwa pokha, koma mumtima mwawo muli chiwembu. Komwe wachoka osamatsekako ndi mwala, koma mayani. -Ndi bwino kumasiyana bwino ndi anthu ukamachoka pamudzi, chifukwa tsiku lina udzabwererako. Kondwerekondwere samatha, kumbuka zili kudza. -Posangalala pamafunika kumaganizira zam’tsogolo. Konsekonse mpeni wansengwa. -Tiyenera kumachitirana zabwino kapena kumathandizana. 84