Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 83

Miyambi ya Patsokwe chake. Ndiye kachizindikiro kangachepe bwanji tizikhala nako tcheru. Kaulamchokero adaika phale padzuwa. -Tikamafuna kuchoka pamalo kapena pamudzi, tisamachoke ti- tawonongapo chifukwa mawa tidzafuna kubwererakonso. Kaulere sikachepa. -Tiyenera kumathokoza tikapatsidwa zinthu ngakhale zitakhala zochepa. Kawalewale adapweteka m’dayeretsa. -Tizichenjera ndi zosangalatsa zomwe pamapeto pake zimabw- eretsa mavuto. Kawerewere kadautsa njovu. -Ngati sitisamala, chinthu chaching’ono chitha kubutsa mavuto aakulu monga mmene kamoto kakang’ono kamayatsira nkhalango. Kayenda m’sana kapenya malowo. -Ngati pamlandu munthu akuyankhula m’maso muli gwa, ndiye kuti ali ndi podalira. Kayenda m’sana katamanda maoloko. -Tizidalira abale ndi alongo athu chifukwa ndi amene amadza- tigwira dzanja tikadzakumana ndi mavuto. Khalidwe silifanana ndi kudziwika. -Munthu akhoza kukhala wodziwika koma wopanda khalidwe. Khama lidaphetsa mbewa zapachulu. -Tikafuna kupeza chinthu tiyenera kuchita khama kwambiri. Koma tikachita khamalo, tizidyerera thukuta lathu. Khasu la apongozi lopanda chimbetete. -Munthu sungagwiritse ntchito chinthu chobwereka m’mene 82