Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 82

Miyambi ya Patsokwe Kapinji mayendayenda kasiya anzake asewera. -Kuchenjeretsa kapena kuyendayenda popanda zifukwa zomve- ka kumabweretsa mavuto. Kaponda mvichili. -Mawuwa akutanthauza mawu abodza ochokera kwa munthu amene zokamba zake sizimakhala zoona. Kapota nyanga, n’kulinga katachenjera. -Ngati nyama yafika poyamba kupota nyanga ndiye kuti inali yochenjera pothawa alenje ndipo imakhala ndi moyo wautali. Munthu amene wafika pokalamba ndiye kuti anapewa zinthu zambiri zomwe zikanatha kuwononga moyo wake. Kapusa n’kamake, kopanda amake kachenjera. -Anthu ambiri amene amakhala ndi makolo awo amapusa. Amachenjera makolo awo akamwalira. Umasiye umaphunzitsa zambiri. Kasiyagoli. -Mawuwa amanena za munthu yemwe amanena bodza lotsekemera n’cholinga choti zinthu zimuyendere bwino. An- ganenedwenso ponena za munthu amene wapulumuka pamlan- du chifukwa chodziwa kuyankhula. Kasule wa m’chikho cholimba kuwawa. -Munthu amene amachita zoipa amakumana ndi mavuto oopsa ngati mmene chikho cholimba chimatulutsira madzi kapena mowa wowawa. Kathabwalika thumba lamwala lokanika kusoka. -Awa ndi mawu okokomeza onena za munthu waukamberem- bere, tambwali. Kati deru kaopsa mlenje. -Kanthu sikachitika popanda chifukwa kapena choyambitsa 81