Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 80

Miyambi ya Patsokwe Kanthu kali m’mwayi, m’kamwini mnzanga wadya phiko. -Anthu ena amakhala ndi mwayi pagulu kapena pamudzi. Kanthu kali munye. -Munthu umadziwa zinthu kuchokera kwa ena. Mwachitsanzo, kuti udziwe nkhani inayake zimadalira kuti ena akuuze. Kanthu kalikonse m’chifuniro, Buluzi anakana bweya. -Munthu aliyense ayenera kumakhala ndi ufulu wochita zimene akufuna. Kanthu kandikhalira pamphuno. -Mawuwa amanenedwa munthu akakumana ndi mavuto omwe palibe chimene angachite kuti awathetse. Zimakhala ngati vuto- lo lamuyandikira kwambiri moti palibe chimene angachite kuti alimbane nalo. Kanthu kavumbu ndi m’manja, m’magona mosambasamba. -Pamoyo wathu tizikhala okonzeka kukumana ndi zilizonse zotigwera, monga matenda komanso zina zosayembekezereka. Kanthu koyambira sikachedwa kuoneka. -Anzathu akatilangiza pa nkhani inayake tiyenera kuchita kapena kusintha, tisamazengereze chifukwa zimadzaonekadi. Kanthu n’kako uvundukura nupenya. -Zinthu zako suziopa. Ukhoza kuchita nazo chilichonse chimene ukufuna. Kanthu n’kako, kamwini kadalira madzi. -Zinthu zako suziopa. Ukhoza kuchita nazo chilichonse chimene ukufuna popanda kuopa aliyense. Kanthu n’kako, kamwini n’kamwini. -Zinthu zako suziopa. Ukhoza kuchita nazo chilichonse chimene ukufuna popanda kuopa aliyense. 79