Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 79

Miyambi ya Patsokwe Kangaonde kalira mtembo. -Munthu aliyense ayenera kumalemekezedwa, osayang’ana mmene alili. Kangaonde kamakoma ndi mchere. -Zinthu zooneka monyozeka zimatha kukhala zosililika chifu- kwa chowonjezera tina n’tina. Kankhuku kachilendo sikachedwa kugwidwa. -Chinthu kapena munthu wachilendo pamalo nthawi zambiri amadedwa. Chilichonse chikalakwika amati wachititsa kapena wachita ndi iyeyo. Kansalu kakafupi, malamulo tho! -Mwambiwu unayamba chifukwa cha khalidwe la amuna ena omwe amagulira akazi awo nsalu yosakwanira n’kumalongolola kapena kukhazikitsa malamulo ambirimbiri. Osamavuta kwam- biri tikhala ndi zinthu kapena tikachita chinachake. Kanthu kakakhala kako, sikaneneka. -Ngati nkhani ikukukhudza, si chapafupi kuinena. Ambiri zikatero amangokhala du! Kanthu kali kuchala. -Kuti udziwe za chinthu, uyenera kuuzidwa ndi amene aku- chidziwa bwino. Kanthu kali m’makonda Buluzi akhumbira khonde. -Zokonda zimasiyanasiyana, choncho mnzathu akamakonda zi- nazake, tisamuseke chifukwa zokonda zathunso zikhoza kukha- la zoseketsa kwa anthu ena. Kanthu kali m’malira, Kalulu adalilira makutu. -Pofunsira ntchito kapena mbeta munthu azisankha yekha m’malo momusankhira chifukwa makonda amasiyanasiyana. 78