Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 78

Miyambi ya Patsokwe Kandimverere adamva zam’maluwa. -Ngati tikukayika kapena sitikudziwa zoyenera kuchita ndi bwino kufunsa kuti tichite zinthu moyenera. Kangachepe n’kachipongwe. -Tisamaikire kumbuyo munthu wolakwa chifukwa cha msinkhu wake. Si onse amene amachita chilungamo komanso chipongwe sichichepa. Kangachepe n’kang’oma, mkulu saomba chitsa. -Tizikhutitsidwa ndi zomwe tili nazo kapena tapatsidwa. Mwachitsanzo, munthu wopemphetsa samafuna kuti amupatse zodzadza thumba. Kangachepe, fungo n’lamake. -Anthufe timatengera makhalidwe ena kuchokera kwa makolo. Komabe, tiyenera kayesetsa kuchita zomwe tingathe kuti tisinthe makhalidwe oipa. Kangachepe, kako n’kako ndithu, kamwini sakandira. -Kanthu kako ukhoza kukagwiritsa ntchito m’mene ukufunira koma kamwini ayi. Kangakanga adathyola nyani mchira. -Si bwino kumaganiza kuti ukhoza kukwanitsa kuchita chili- chonse wekha chifukwa ukadzapeza mavuto udzasowa wokuthandiza. Kangakanga anathyola nyau. -Si bwino kumaganiza kuti ukhoza kukwanitsa kuchita chili- chonse wekha chifukwa ukadzapeza mavuto udzasowa wokuthandiza. Kangakanga kanakanga. -Si bwino kuti munthu udzikhala wodzikonda kapena woumira chifukwa tsiku lina zikadzakuvuta umadzasowa wokuthandiza. 77