Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 77

Miyambi ya Patsokwe mopupuluma. Kampango woyera kumimba. -Mawuwa amanenedwa ndi munthu amene akukana mlandu ponena kuti, “Ndilibe mlandu ndi munthu chifukwa palibe um- boni wokwanira.” Kamtande alemba pali khola. -Munthu akakhalitsa kapena kuima penapake kwa nthawi yaitali, ndiye kuti akudikira chinachake. Kamtengo kamwana n’kamene amaphera njoka. -Anthu anzeru amatha kulephera kuchita zinthu zing’onoz- ing’ono, amawathandiza ndi anthu amene amaoneka ngati opanda nzeru. Kamtsitsi kadagwetsa abambo. -Osachepetsa tchimo kapena cholakwa. Tiyenera kulapa chifu- kwa lingadzatipezetse mavuto m’tsogolo. Kamwana m’chokere, ukulu n’kuona kako. -Mawuwa amanenedwa pakakhala chakudya chochepa. Ama- sonyeza kuti ngakhale chakudya cha mwana, munthu ukhoza kukhuta. Ndi bwino kumavomereza zinthu zikavuta. Kamwini kalibe nkhoko m’nkhali. -Munthu ukapita kwa eni, sumajijirika mpaka kufika pomauza anthu kuti, “Tisunge chakudya chinachi kuti tidzadye m’mama- wa.” Kapena kumakanganirana nawo zakudya zomwe zinatsala dzulo. Ndi bwino kumakhala munthu woupeza mtima tikakhala kuchilendo. Kandimverere adakanena za m’maluwa. -Zongomva chabe sizikhutiritsa. Pamafunika pakhale umboni womveka bwino, apo ayi ndiye umafunika kupita komweko kuti ukadzionere ndi maso ako. 76