Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 73

Miyambi ya Patsokwe Kako n’kako, kamwini sakandira. -Ukabwereka chinthu, sukhala ndi ufulu wochigwiritsa ntchito mmene ukufunira. Ngati ukufuna kumagwiritsa ntchito chinthu momasuka, ndiye ungachite bwino kungopeza chako. Kako ndi ako kali m’mimba, kali padera si kako. -Munthu uziwerengera chimene uli nacho, osati chomwe uku- ganiza kuti ungadzakhale nacho. Kako ndi ako wadya. -Si bwino kutenga zinthu zimene si zako. Chomwe munthu wadya ndiye chako chenicheni chifukwa palibe angakulande. Kako sikanunkha. -Umateteza abale ako komanso anzako. Anthu akamawanenera zoipa, umawakometsera ngakhale zitakhala kuti amachitadi zin- thuzo. Kakonda mnzako mlekere, mawa kakonda iwe. -Osachita nsanje ndi zinthu kapena mwayi wa ena, mawa ukho- za kudzakhala mwayi wako. Kakudza kokha kamalaula. -Kuti upeze chinthu chabwino umayenera kuchivutikira. Chin- thu chongobwera chokha n’chosadalirika. Choncho, si bwino kukhala munthu waulesi. Kale silibwerera. -N’kupanda mnzeru kumalilira zakale. Ndi nzeru kumaganizira za mawa mmalo momataya nthawi kuganizira zinthu zomwe zinachitika kale ndipo sungazisinthe ngakhale pang’ono. Kali kokha n’kanyama, tili awiri n’tianthu. -Kukhala awiri si mantha, mumathandizana nzeru. Koma mun- thu wokonda kuyenda yekha kapena kuchita zinthu payekha 72