Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 72

Miyambi ya Patsokwe chake m’pofunika kumasamala ndi zimene timayankhula kuopa kuyambitsa chipwirikiti. Kagwa m’maso ndi kako. -Osamawerengera zinthu zimene sunazilandire, mwina sizib- wera. Chomwe uli nacho ndiye chako. Kagwa m’maso tola. -Mwambiwu ukunena za wakuba amene amatenga chilichonse chomwe waona. Kaitana kavula, ukachedwa ukakapeza katabopha. -Ukaitanidwa umafunika kupita mofulumira, chifukwa ukachedwa umakapeza zimene amakuitanirazo zitatha. Kuchita zinthu panthawi yake komanso mosazengereza pamene wai- tanidwa n’kofunika kwambiri. Ukachedwa umakapeza zatha kale. Kaitana kavula, ukachedwa upeza katavala. -Ukaitanidwa umafunika kupita mofulumira, chifukwa ukachedwa umakapeza zimene amakuitanirazo zitatha. Kuchita zinthu panthawi yake komanso mosazengereza pamene wai- tanidwa n’kofunika kwambiri. Ukachedwa umakapeza zatha kale. Kakachenjeretsa sikanona. -Nthawi zambiri amene amakonda kuyankhulayankhula kapena ochenjeretsa amakhala opanda nzeru. Chimodzimodzinso okon- gola, amangokongola nkhope koma n’kukhala opanda nzeru kapena opanda khalidwe. Kako n’kako, kamwini katukwanitsa. -Kanthu kako ukhoza kukagwiritsa ntchito m’mene ukufunira koma kamwini ayi. 71