Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 70
Miyambi ya Patsokwe
Kachipande katherere kamakoma n’kuyenderana.
-Anthu amene amakhala bwino amafunika kumayenderana ko-
manso kupatsana zinthu. Amafunikanso kuthandizana zikavuta,
m’malo momangoyembekezera kuti munthu m’modzimodzi
azitichitira zabwino. Mnzako akukuchitira zabwino nawenso
ndi bwino kumuchitira zabwino.
Kachirombo kofula m’njira katama mano.
-Munthu aliyense pamene akuyamba kuchita chinthu, monga
banja kapena kulima munda, amafunika kuona kaye ngati an-
gakwanitse. Amafunikanso kuona ngati ali ndi zonse zofunika
kuti akwaniritse chinthucho. Mwachitsanzo, si bwino kulilowa
banja ukumadalira ena kuti adzakuthandiza kapena kumabere-
ka ana ukuwerengera kuti amalume adzawaphunzitsa.
Kadapota nyanga kamadya ndi mvumbi.
-Tiziganizira za tsogolo lathu. Kanyama kena kankaopa mvula
ndipo sikankatuluka kupita kukadya moti kanaonda. Ndiye
mvula itatha kanapita kukaba chakudya ndipo kanaphedwa. Ka-
kanadya bwino nthawi ya mvula bwenzi kali ndi moyo nthawi
yosowa chakudya.
Kaduka ka chinangwa.
-Mawuwa amatanthauza nsanje. Chifukwa cha nsanje,
chinangwa chikazulidwa sichiphukanso kuopa kuti anthu anga-
bwerenso ndi kudzathyola masamba ake kuti akapange ndiwo
(chigwada) kapena kudzachizulanso.
Kaduwa kokongola kamakopa Njuchi.
-Anthu amatengeka ndi zimene akuona. Mwachitsanzo, amuna
amakopeka ndi kukongola n’chifukwa chake akazi
amadziphoda kuti akope njuchi.
Kadya n’kena mbiri n’nja Khoswe.
-Pali anthu ena chifukwa cha maonekedwe awo anthu
69