Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 69

Miyambi ya Patsokwe Kachaje sikachepa, kachepa n’kamalonda. -Tiyenera kuthokoza tikapatsidwa zinthu mwaulere ngakhale zitakhala zochepa. Koma ngati tagula ndipo zinthuzo sizinakwane pa mlingo wake, tiyenera kudandaula. Kachepa alibe bwalo, ali ndi bwalo ndi kangachepe. -Si bwino kumaderera zimene wangopatsidwa, kumangothoko- za. Kachepa kayenda, kakafa n’kophika. -Pochita cholakwa munthu umaona ngati chaching’ono. Koma chikaululika chimasanduka chachikulu komanso chochititsa manyazi. Kachepa n’kovala, kakudya sikachepa. -Chovala chimodzi simungathe kuvala anthu awiri nthawi imodzi. Koma chakudya ngakhale chitachepa bwanji mukhoza kugawana. Mawuwa amanenedwa poitanira ena kuti adzadye nawo chakudya. Kachepa, n’kuona msandulizo. -Vuto limachepa ngati tili ndi ena omwe angatithandize. Kachepera maso, kamwa lilanda. -Pali zinthu zina monga chakudya, milandu, zomwe poziona zimakhala ngati zochepa koma kuti tizidye kapena kuzikamba zimakhala zazikulu. Tisamaderere zakudya kapena kunyozetsa nkhani. Kachinyiza anang’amba thumba. -Si bwino kukakamiza wina kuchita chinthu chomwe sakufuna, chifukwa mapeto ake timapezeka tawononga, m’malo mokonza. Kachinziri kamatupa patsala lake. -Munthu amamasuka akakhala kwawo. Akhoza kudya kapena kuchita zinthu zomwe kukanakhala kuchilendo sakanachita. 68