Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 66

Miyambi ya Patsokwe wakuba ali m’modzi yekha. Kulakwa kwa munthu wina kukho- za kukhudza anthu ena. Ili ndi amake simagwa m’mbuna. -Anthu amene amalangiza ana awo ndipo anawo namvera malangizo awo, kawirikawiri amakula bwino popanda mavuto ambiri. Iliko nja usiku, mkamwini anajiwa dzanja. -Si bwino kuyembekezera zinthu chifukwa zikapanda kubwera timadzagwira njakata. Imfa ilibe odi. -Imfa siipanganika, imabwera nthawi yosayembekezereka. Choncho, timafunika kukonza moyo wathu wauzimu kuti tikhale ndi tsogolo labwino. Imfa siisankha, imatenga mkulu ndi mwana yemwe. -Aliyense azikhala wokonzeka kuti tsiku lina adzamwalira. Imfa siona nkhope. -Imfa potenga munthu siyang’ana kuti uyu ndi ndani. Imfa sithawika. -Ngakhale munthu atachita zotani kuti asamwalire, mapeto ake amafabe. Ine-ine sin’theka pofula uchi. -Si bwino kumangomva zathu zokha komanso kumamva malangizo a ena ndinso kugawana nawo zomwe tili nazo. Um- bombo suthandiza. Ine-ine, sindim’tenga. -Si bwino kumachita zinthu modzikonda pamalo, mapeto ake umataya mwayi wopeza zabwino. Anthu sagwirizana ndi mun- thu amene amachita zinthu modzikuza. 65