Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 65

Miyambi ya Patsokwe Idakula nyanga poopa malunje. -Kuti munthu akule ndi moyo ndiponso makhalidwe abwino, ayenera kumalemekeza akuluakulu ndiponso kumadzisamalira monga nyama imene imakula nyanga poopa kuyenda m’nk- halango. Ikachuluka pakamwa, siipenya pathumba. -Pantchito pakachuluka anthu, ntchito siyenda, mmalo mwake zimachuluka ndi nkhani. Ikadza njala, umadya kontho. -Munthu ukakhala pamavuto umachita zinthu zomwe sungachite uli pamtendere. Ikadza njala, usamataye gaga. -Munthu aliyense amafunika kusamalira chuma chake, chifukwa akachiwononga, tsiku lina amadzachifuna akadzakhala pa- mavuto. Ikadza njala, usamataye mtondo. -Munthu aliyense amafunika kusamalira chuma chake, chifukwa akachiwononga, tsiku lina amadzachifuna akadzakhala pa- mavuto. Ikakuthawa imawawa nsuzi. -Munthu wina anagwira Njiwa ndipo anasangalala kwambiri chifukwa ankadziwa kuti nsima ya tsiku limenelo ikayenda. Ko- ma ali mkati moganiza zimenezi, Njiwayo inamupulumuka n’kuthawa. Munthuyo anapsa mtima n’kuyamba kuikuwira Njiwayo n’kumaiuza kuti, “Iweeeeeeeee, umawawa msuzi!” Phunziro ndi lakuti osamanyoza chinthu chikapita. Ikaola imodzi, zawola zonse. -Pamudzi munthu akakhala wamakhalidwe oipa monga waku- ba, anthu amangoti mudzi wonse ndi wa anthu akuba ngakhale 64